Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 26:8-12 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

8. Yehova, ndikonda cikhalidwe ca nyumba yanu,Ndi malo akukhalamo ulemerero wanu.

9. Musandicotsere mzimu wanga pamodzi ndi olakwa,Kapena moyo wanga pamodzi ndi anthu okhetsa mwazi:

10. Amene m'manja mwao muli mphulupulu,Ndi dzanja lao lamanja ladzala ndi zokometsera mlandu.

11. Koma ine, ndidzayenda m'ungwiro wanga;Mundiombole, ndipo ndicitireni cifundo.

12. Phazi langa liponda pacidikha:M'masonkhano ndidzalemekeza Yehova.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 26