Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 26:5-11 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

5. Ndidana nao msonkhano wa ocimwa,Ndipo sindidzakhala nao pansi ocita zoipa.

6. Ndidzasamba manja anga mosalakwa;Kuti ndizungulire guwa la nsembe lanu, Yehova:

7. Kuti ndimveketse mau a ciyamiko,Ndi kulalikira nchito zanu zonse zozizwa.

8. Yehova, ndikonda cikhalidwe ca nyumba yanu,Ndi malo akukhalamo ulemerero wanu.

9. Musandicotsere mzimu wanga pamodzi ndi olakwa,Kapena moyo wanga pamodzi ndi anthu okhetsa mwazi:

10. Amene m'manja mwao muli mphulupulu,Ndi dzanja lao lamanja ladzala ndi zokometsera mlandu.

11. Koma ine, ndidzayenda m'ungwiro wanga;Mundiombole, ndipo ndicitireni cifundo.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 26