Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 26:1-8 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Mundiweruze, Yehova, pakuti ndayenda m'ungwiro wanga:Ndipo ndakhulupirira Yehova, sindidzaterereka.

2. Mundiyesere, Yehova, ndipo mundisunthe;Yeretsani imso zanga ndi mtima wanga.

3. Pakuti cifundo canu ciri pamaso panga;Ndipo ndayenda m'coona canu.

4. Sindinakhala pansi ndi anthu acabe;Kapena kutsagana nao anthu otyasika.

5. Ndidana nao msonkhano wa ocimwa,Ndipo sindidzakhala nao pansi ocita zoipa.

6. Ndidzasamba manja anga mosalakwa;Kuti ndizungulire guwa la nsembe lanu, Yehova:

7. Kuti ndimveketse mau a ciyamiko,Ndi kulalikira nchito zanu zonse zozizwa.

8. Yehova, ndikonda cikhalidwe ca nyumba yanu,Ndi malo akukhalamo ulemerero wanu.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 26