Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 25:6-19 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

6. Kumbukilani, Yehova, nsoni zanu ndi cifundo canu;Pakuti izi nza kale lonse,

7. Musakumbukile zolakwa za ubwana wanga kapena zopikisana nanu:Mundikumbukile monga mwa cifundo canu,Cifukwa ca ubwino wanu, Yehova.

8. Yehova ndiye wabwino ndi wolunjika mtima:Cifukwa cace adzaphunzitsa olawa za njira.

9. Adzawatsogolera ofatsa m'ciweruzo:Ndipo adzaphunzitsa ofatsa njira yace.

10. Mayendedwe onse a Yehova ndiwo cifundo ndi coonadi,Kwa iwo akusunga pangano lace ndi mboni zace.

11. Cifukwa ca dzina lanu, Yehova,Ndikhululukireni kusakaza kwanga, pakuti ndiko kwakukuru.

12. Munthuyo wakuopa Yehova ndani?Adzamlangiza iye njira adzasankheyo.

13. Moyo wace udzakhala mokoma;Ndi mbumba zace zidzalandira dziko lapansi.

14. Cinsinsi ca Yehova ciri kwa iwo akumuopa Iye;Ndipo adzawadziwitsa pangano lace.

15. Maso anga alinga kwa Yehova kosaleka;Pakuti Iye adzaonjola mapazi anga m'ukonde.

16. Ceukirani ine ndipo ndicitireni cifundo;Pakuti ndiri woungumma ndi wozunzika.

17. Masautso a mtima wanga akula:Munditurutse m'zondipsinja.

18. Penyani mazunzo anga ndi zabvuta zanga;Ndipo khululukirani zolakwa zanga zonse.

19. Penyani adani anga, popeza acuruka;Ndipo andida ndi udani waciwawa.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 25