Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 25:1-7 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndikweza moyo wanga kwa Inu, Yehova.

2. Mulungu wanga, ndakhulupirira Inu,Ndisacite manyazi;Adani anga asandiseke ine.

3. Inde, onse akuyembekezera Inu sadzacita manyaziAdzacita manyazi iwo amene acita monyenga kopanda cifukwa.

4. Mundidziwitse njira zanu, Yehova;Mundiphunzitse mayendedwe anu.

5. Munditsogolere m'coonadi canu, ndipo mundiphunzitse;Pakuti Inu ndinu Mulungu wa cipulumutso canga;Inu ndikuyembekezerani tsiku lonseli.

6. Kumbukilani, Yehova, nsoni zanu ndi cifundo canu;Pakuti izi nza kale lonse,

7. Musakumbukile zolakwa za ubwana wanga kapena zopikisana nanu:Mundikumbukile monga mwa cifundo canu,Cifukwa ca ubwino wanu, Yehova.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 25