15. Mphamvu yanga yauma ngati phale;Ndi lilime langa likangamira ku nsaya zanga;Ndipo mwandifikitsa ku pfumbi la imfa.
16. Pakuti andizinga agaru:Msonkhano wa oipa wanditsekereza;Andiboola m'manja anga ndi m'mapazi anga.
17. Ndikhoza kuwerenga mafupa anga onse;Iwo ayang'ana nandipenyetsetsa ine:
18. Agawana zobvala zanga,Nalota maere pa malaya anga,
19. Koma Inu, Yehova, musakhale kutari;Mphamvu yanga Inu, mufulumire kundithandiza.