Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 22:15-19 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

15. Mphamvu yanga yauma ngati phale;Ndi lilime langa likangamira ku nsaya zanga;Ndipo mwandifikitsa ku pfumbi la imfa.

16. Pakuti andizinga agaru:Msonkhano wa oipa wanditsekereza;Andiboola m'manja anga ndi m'mapazi anga.

17. Ndikhoza kuwerenga mafupa anga onse;Iwo ayang'ana nandipenyetsetsa ine:

18. Agawana zobvala zanga,Nalota maere pa malaya anga,

19. Koma Inu, Yehova, musakhale kutari;Mphamvu yanga Inu, mufulumire kundithandiza.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 22