10. Cibadwire ine anandisiyira Inu:Kuyambira kwa mai wanga Mulungu wanga ndinu.
11. Musandikhalire kutali; pakuti nsautso iri pafupi:Pakuti palibe mthandizi.
12. Ng'ombe zamphongo zambiri zandizinga:Mphongo zolimba za ku Basana zandizungulira,
13. Andiyasamira m'kamwa mwao,Ngati mkango wozomola ndi wobangula.
14. Ndathiridwa pansi monga madzi,Ndipo mafupa anga onse anaguluka:Mtima wanga ukunga sera; Wasungunuka m'kati mwa matumbo anga,
15. Mphamvu yanga yauma ngati phale;Ndi lilime langa likangamira ku nsaya zanga;Ndipo mwandifikitsa ku pfumbi la imfa.
16. Pakuti andizinga agaru:Msonkhano wa oipa wanditsekereza;Andiboola m'manja anga ndi m'mapazi anga.
17. Ndikhoza kuwerenga mafupa anga onse;Iwo ayang'ana nandipenyetsetsa ine:
18. Agawana zobvala zanga,Nalota maere pa malaya anga,
19. Koma Inu, Yehova, musakhale kutari;Mphamvu yanga Inu, mufulumire kundithandiza.