Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 21:1-8 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Yehova, adzasekera mfumu mu mphamvu yanu;Adzakondwera kwakukuru m'cipulumutso canu!

2. Mwampatsa iye cikhumbo ca mtimawace,Ndipo simunakana pempho la milomo yace.

3. Pakuti mumkumika iye ndi madalitso okoma:Muika korona wa golidi woyengetsa pamutu pace.

4. Anakupemphani moyo, mwampatsa iye;Mwamtalikitsira masiku ku nthawi za nthawi.

5. Ulemerero wace ngwaukuru mwa cipulumutso canu:Mumcitira iye ulemu ndi ukulu.

6. Pakuti mumuikira madalitso ku nthawi zonse;Mumkondweretsa ndi cimwemwe pankhope panu.

7. Pakuti mfumu akhulupirira Yehova,Ndipo mwa cifundo ca Wam'mwambamwamba sadzagwedezeka iye,

8. Dzanja lanu lidzapeza adani anu onse:Dzanja lanu lamanja lidzapeza iwo akuda Inu.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 21