Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 2:4-12 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

4. Wokhala m'mwambayo adzaseka;Ambuye adzawanyoza.

5. Pomwepo adzalankhula nao mu mkwiyo wace,Nadzawaopsa m'ukali wace:

6. Koma Ine ndadzoza mfumu yangaPa Ziyoni, phiri langa loyera.

7. Ndidzauza za citsimikizo:Yehova ananena ndiIne, Iwe ndiwe Mwana wanga;Ine lero ndakubala.

8. Undifunse, ndipo ndidzakupatsa amitundu akhale colowa cako,Ndi malekezero a dziko lapansi akhale ako ako.

9. Udzawatyola ndi ndodo yacitsulo;Udzawaphwanya monga mbiya yawoumba.

10. Tsono, mafumu inu, citani mwanzeru:Langikani, oweruza inu a dziko lapansi.

11. Tumikirani Yehova ndi mantha,Ndipo kondwerani ndi cinthenthe.

12. Mpsompsoneni Mwanayo, kuti angakwiye, ndipo mungatayike m'njira,Ukayaka pang'ono pokha mkwiyo wace.Odala onse akumkhulupirira Iye.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 2