Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 19:9-14 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

9. Kuopa Yehova kuli mbe, kwakukhalabe nthawi zonse:Maweruzo a Yehova ali oona, alungama konse konse.

10. Ndizo zifunika koposa golidi, inde, golidi wambiri woyengetsa:Zizuna koposa uci ndi zakukha za zisa zace,

11. Ndiponso kapolo wanu acenjezedwa nazo:M'kuzisunga izo muli mphotho yaikuru.

12. Adziwitsa zolowereza zace ndani?Mundimasule kwa zolakwa zobisika.

13. Ndiponso muletse kapolo wanu pa zodzitama;Zisacite ufumu pa ine: pamenepo ndidzakhala wangwiro,Ndi wosacimwa colakwa cacikuru.

14. Mau a m'kamwa mwanga ndi maganizo a m'mtima wanga abvomerezeke pamaso panu,Yehova, thanthwe langa, ndi Mombolo wanga,

Werengani mutu wathunthu Masalmo 19