9. Kuopa Yehova kuli mbe, kwakukhalabe nthawi zonse:Maweruzo a Yehova ali oona, alungama konse konse.
10. Ndizo zifunika koposa golidi, inde, golidi wambiri woyengetsa:Zizuna koposa uci ndi zakukha za zisa zace,
11. Ndiponso kapolo wanu acenjezedwa nazo:M'kuzisunga izo muli mphotho yaikuru.
12. Adziwitsa zolowereza zace ndani?Mundimasule kwa zolakwa zobisika.
13. Ndiponso muletse kapolo wanu pa zodzitama;Zisacite ufumu pa ine: pamenepo ndidzakhala wangwiro,Ndi wosacimwa colakwa cacikuru.
14. Mau a m'kamwa mwanga ndi maganizo a m'mtima wanga abvomerezeke pamaso panu,Yehova, thanthwe langa, ndi Mombolo wanga,