Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 19:2-7 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

2. Usana ndi usana ucurukitsa mau,Ndipo usiku ndi usiku uonetsa nzeru.

3. Palibe cilankhulidwe, palibe mau;Liu lao silimveka.

4. Muyeso wao wapitirira pa dziko lonse lapansi,Ndipo mau ao ku malekezero a m'dziko muli anthu.Iye anaika hema la dzuwa m'menemo,

5. Ndipo liri ngati mkwati wakuturuka m'cipinda mwace,Likondwera ngati ciphona kuthamanga m'njira.

6. Kuturuka kwace lituruka kolekezera thambo,Ndipo kuzungulira kwace lifikira ku malekezero ace:Ndipo kulibe kanthu kobisalira kutentha kwace.

7. Malamulo a Yehova ali angwiro, akubwezera moyo;Mboni za Yehova ziri zokhazikika, zakuwapatsa opusa nzeru;

Werengani mutu wathunthu Masalmo 19