Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 18:4-9 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

4. Zingwe za imfa zinandizinga,Ndipo mitsinje ya zopanda pace inandiopsa.

5. Zingwe za manda zinandizinga:Misampha ya imfa inandifikira ine.

6. M'kusauka kwanga ndinaitana Yehova,Ndipo ndinakuwira Mulungu wanga;Mau anga anawamva m'Kacisi mwace,Ndipo mkuwo wanga wa pankhope pace unalowa m'makutu mwace.

7. Pamenepo linagwedezeka, ndi kutenthemera dziko lapansi.Ndi maziko a mapiri ananjenjemeraNagwedezeka, pakuti anakwiya iyeyo.

8. Unakwera utsi woturuka m'mphuno mwace:Ndi moto wa m'kamwa mwace unanyeka:Nuyakitsa makara.

9. Ndipo Iye anaweramitsa thambo, natsika;Ndipo pansi pa mapazi ace panali mdima bii.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 18