Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 18:36-47 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

36. Mwandipondetsa patali patali,Sanaterereka mapazi anga.

37. Ndidzalondola adani anga, ndi kuwapeza:Ndipo sindidzabwerera asanathe psiti.

38. Ndidzawapyoza kuti sangakhoze kuuka:Adzagwa pansi pa mapazi anga,

39. Pakuti mwaudizingiza mphamvu m'cuuno ku nkhondoyo:Mwandigonjetsera amene andiukira.

40. Ndipo adani anga mwawalozetsa m'mbuyo kwa ine,Kuti ndipasule ondidawo.

41. Anapfuula, koma panalibewopulumutsa;Ngakhale kwa Yehova, koma sanawabvomereza.

42. Pamenepo ndinawapera ngati pfumbi la kumphepo;Ndinawakhuthula ngati matope a pabwalo.

43. Mwandipulumutsa pa zolimbana nane za anthu;Mwandiika mutu wa amitundu;Mtundu wa anthu sindinaudziwa udzanditumikira.

44. Pakumva m'khutu za ine adzandimvera:Alendo adzandigonjera monyenga.

45. Alendo adzafota,Nadzaturuka monjenjemera m'ngaka mwao.

46. Yehova ngwa moyo; ndipo lidalitsike thanthwe langa;Nakwezeke Mulungu wa cipulumutso canga:

47. Ndiye Mulungu amene andibwe, zerera cilango,Nandigonjetsera mitundu ya anthu.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 18