Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 18:32-37 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

32. Mulungu ndiye wondizingiza mphamvu m'cuuno,Nakonza njira yanga ikhale yangwiro.

33. Alinganiza mapazi anga ngati a nswala:Nandiimitsa pamsanje panga.

34. Aphunzitsa manja anga agwire nkhondo;Kuti walifuka uta wamkuwa ndi manja anga.

35. Ndipo mwandipatsa cikopa ca cipulumutso canu:Ndipo dzanja lamanja lanu landigwiriziza,Ndipo cifatso canu candikuza ine.

36. Mwandipondetsa patali patali,Sanaterereka mapazi anga.

37. Ndidzalondola adani anga, ndi kuwapeza:Ndipo sindidzabwerera asanathe psiti.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 18