Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 18:31-40 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

31. Pakuti Mulungu ndani wosati Yehova?Ndipo thanthwe ndani wosati Mulungu wathu?

32. Mulungu ndiye wondizingiza mphamvu m'cuuno,Nakonza njira yanga ikhale yangwiro.

33. Alinganiza mapazi anga ngati a nswala:Nandiimitsa pamsanje panga.

34. Aphunzitsa manja anga agwire nkhondo;Kuti walifuka uta wamkuwa ndi manja anga.

35. Ndipo mwandipatsa cikopa ca cipulumutso canu:Ndipo dzanja lamanja lanu landigwiriziza,Ndipo cifatso canu candikuza ine.

36. Mwandipondetsa patali patali,Sanaterereka mapazi anga.

37. Ndidzalondola adani anga, ndi kuwapeza:Ndipo sindidzabwerera asanathe psiti.

38. Ndidzawapyoza kuti sangakhoze kuuka:Adzagwa pansi pa mapazi anga,

39. Pakuti mwaudizingiza mphamvu m'cuuno ku nkhondoyo:Mwandigonjetsera amene andiukira.

40. Ndipo adani anga mwawalozetsa m'mbuyo kwa ine,Kuti ndipasule ondidawo.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 18