Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 18:24-32 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

24. Ndimo anandisudzulira Yehova monga mwa cilungamo canga,Monga mwa kusisira kwa manja anga pamaso pace.

25. Pa wacifundo mukhala wacifundoPa mumthu wangwiro mukhala wangwiro;

26. Pa woyera mtima mukhala woyera mtima;Pa wotsutsatsutsa mukhala wotsutsana naye.

27. Pakuti Inu muwapulumutsa anthu aumphawi;Koma maso okweza muwatsitsa.

28. Pakuti Inu muyatsa nyali yanga;Yehova, Mulungu wanga, aunikira mdima wanga.

29. Pakuti mwa Inu ndipyola khamu la anthu;Ndipo mwa Mulungu wanga ndilumphira linga.

30. Mulungu ndiyewangwiro m'njira zace;Mau a Yehova ngoyengeka; Ndiye cikopa ca onse okhulupirira Iye.

31. Pakuti Mulungu ndani wosati Yehova?Ndipo thanthwe ndani wosati Mulungu wathu?

32. Mulungu ndiye wondizingiza mphamvu m'cuuno,Nakonza njira yanga ikhale yangwiro.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 18