Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 18:22-26 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

22. Pakuti maweruzo ace onse anali pamaso panga,Ndipo malemba ace sindinawacotsa kwa ine.

23. Ndipo ndinakhala wangwiro ndi iye,Ndipo ndinadzisunga wosacita coipa canga.

24. Ndimo anandisudzulira Yehova monga mwa cilungamo canga,Monga mwa kusisira kwa manja anga pamaso pace.

25. Pa wacifundo mukhala wacifundoPa mumthu wangwiro mukhala wangwiro;

26. Pa woyera mtima mukhala woyera mtima;Pa wotsutsatsutsa mukhala wotsutsana naye.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 18