Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 148:1-10 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Haleluya.Lemekezani Yehova kocokera kumwamba;Mlemekezeni m'misanje.

2. Mlemekezeni, angelo ace onse;Mlemekezeni, makamu ace onse.

3. Mlemekezeni, dzuwa ndi mwezi;Mlemekezeni, nyenyezi zonse zaunikira.

4. Mlemekezeni, m'mwambamwamba,Ndi madzi inu, a pamwamba pa thambo.

5. Alemekeze dzina la Yehova;Popeza analamulira, ndipo zinalengedwa.

6. Anazikhazikanso ku nthawi za nthawi;Anazipatsa cilamulo cosatumphika.

7. Lemekezani Yehova kocokera ku dziko lapansi,Zinsomba inu, ndi malo ozama onse;

8. Moto ndi matalala, cipale cofewa ndi nkhungu;Mphepo ya namondwe, yakucita mau ace;

9. Mapiri ndi zitunda zonse;Mitengo yazipatso ndi yamikungudza yonse:

10. Nyama za kuthengo ndi zoweta zonse;Zokwawa, ndi mbalame zakuuluka;

Werengani mutu wathunthu Masalmo 148