Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 147:7-20 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

7. Yamikani Yehova ndi kuthira mang'ombe;Myimbireni Mulungu wathu zamlemekeza pazeze:

8. Amene aphimba thambo ndi mitambo,Amene akonzera mvula nthaka,Amene aphukitsa msipu pamapiri.

9. Amene apatsa zoweta cakudya cao,Ana a khungubwi alikulira.

10. Mphamvu ya kavalo siimkonda:Sakondwera nayo miyendo ya munthu.

11. Yehova akondwera nao akumuopa Iye,Iwo akuyembekeza cifundo cace.

12. Yerusalemu, lemekezani Yehova;Ziyoni, lemekezani Mulungu wanu.

13. Popeza analimbitsa mipiringidzo ya zitseko zanu:Anadalitsa ana anu m'kati mwanu.

14. Ndiyeamene akhalitsamalireanu mumtendere;Akukhutitsani ndi tirigu wakuca bwino.

15. Atumiza lamulo lace ku dziko lapansi;Mau ace athamanga liwiro.

16. Apatsa cipale cofewa ngati ubweya;Awaza cisanu ngati phulusa.

17. Aponya matalala ace ngati zidutsu:Adzaima ndani pa kuzizira kwace?

18. Atumiza mau ace nazisungunula;Aombetsa mphepo yace, ayenda madzi ace.

19. Aonetsa mau ace kwa Yakobo;Malemba ace, ndi maweruzo ace kwa Israyeli.

20. Sanatero nao anthu amtundu wina;Ndipo za maweruzo ace, sanawadziwa.Haleluya.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 147