Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 147:6-15 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

6. Yehova agwiriziza ofatsa;Atsitsira oipa pansi.

7. Yamikani Yehova ndi kuthira mang'ombe;Myimbireni Mulungu wathu zamlemekeza pazeze:

8. Amene aphimba thambo ndi mitambo,Amene akonzera mvula nthaka,Amene aphukitsa msipu pamapiri.

9. Amene apatsa zoweta cakudya cao,Ana a khungubwi alikulira.

10. Mphamvu ya kavalo siimkonda:Sakondwera nayo miyendo ya munthu.

11. Yehova akondwera nao akumuopa Iye,Iwo akuyembekeza cifundo cace.

12. Yerusalemu, lemekezani Yehova;Ziyoni, lemekezani Mulungu wanu.

13. Popeza analimbitsa mipiringidzo ya zitseko zanu:Anadalitsa ana anu m'kati mwanu.

14. Ndiyeamene akhalitsamalireanu mumtendere;Akukhutitsani ndi tirigu wakuca bwino.

15. Atumiza lamulo lace ku dziko lapansi;Mau ace athamanga liwiro.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 147