Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 147:3-13 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

3. Aciritsa osweka mtima,Namanga mabala ao.

4. Awerenga nyenyezi momwe ziri;Azicha maina zonsezi.

5. Ambuye wathu ndi wamkuru ndi wa mphamvu zambiri;Nzeru yace njosatha.

6. Yehova agwiriziza ofatsa;Atsitsira oipa pansi.

7. Yamikani Yehova ndi kuthira mang'ombe;Myimbireni Mulungu wathu zamlemekeza pazeze:

8. Amene aphimba thambo ndi mitambo,Amene akonzera mvula nthaka,Amene aphukitsa msipu pamapiri.

9. Amene apatsa zoweta cakudya cao,Ana a khungubwi alikulira.

10. Mphamvu ya kavalo siimkonda:Sakondwera nayo miyendo ya munthu.

11. Yehova akondwera nao akumuopa Iye,Iwo akuyembekeza cifundo cace.

12. Yerusalemu, lemekezani Yehova;Ziyoni, lemekezani Mulungu wanu.

13. Popeza analimbitsa mipiringidzo ya zitseko zanu:Anadalitsa ana anu m'kati mwanu.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 147