Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 147:16-20 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

16. Apatsa cipale cofewa ngati ubweya;Awaza cisanu ngati phulusa.

17. Aponya matalala ace ngati zidutsu:Adzaima ndani pa kuzizira kwace?

18. Atumiza mau ace nazisungunula;Aombetsa mphepo yace, ayenda madzi ace.

19. Aonetsa mau ace kwa Yakobo;Malemba ace, ndi maweruzo ace kwa Israyeli.

20. Sanatero nao anthu amtundu wina;Ndipo za maweruzo ace, sanawadziwa.Haleluya.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 147