Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 147:1-7 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Haleluya;Pakuti kuyimbira zomlemekeza Mulungu wathu nkokoma;Pakuti cikondwetsa ici, cilemekezo ciyenera.

2. Yehova amanga Yerusalemu;Asokolotsa otayika a Israyeli.

3. Aciritsa osweka mtima,Namanga mabala ao.

4. Awerenga nyenyezi momwe ziri;Azicha maina zonsezi.

5. Ambuye wathu ndi wamkuru ndi wa mphamvu zambiri;Nzeru yace njosatha.

6. Yehova agwiriziza ofatsa;Atsitsira oipa pansi.

7. Yamikani Yehova ndi kuthira mang'ombe;Myimbireni Mulungu wathu zamlemekeza pazeze:

Werengani mutu wathunthu Masalmo 147