Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 146:1-7 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Haleluya;Ulemekeze Yehova, moyo wanga,

2. Ndidzalemekeza Yehovam'moyo mwanga;Ndidzayimbira zomlemekeza Mulungu wanga pokhala ndi moyo ine.

3. Musamakhulupirira zinduna,Kapena mwana wa munthu, amene mulibe cipulumutso mwa iye.

4. Mpweya wace ucoka, abwerera kumka ku nthaka yace;Tsiku lomwelo zotsimikiza mtima zace zitayika.

5. Wodala munthu amene akhala naye Mulungu wa Yakobo kuti amthandize,Ciyembekezo cace ciri pa Yehova, Mulungu wace;

6. Amene analenga zakumwamba ndi dziko lapansi,Nyanja ndi zonse ziri m'mwemo;Ndiye wakusunga coonadi kosatha:

7. Ndiye wakucitira ciweruzo osautsika;Ndiye wakupatsa anjala cakudya;Yehova amasula akaidi;

Werengani mutu wathunthu Masalmo 146