Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 145:7-15 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

7. Adzabukitsa cikumbukilo ca ubwino wanu waukuru,Nadzayimbira cilungamo canu.

8. Yehova ndiye wacisomo, ndi wacifundo;Osakwiya msanga, ndi wa cifundo cacikuru.

9. Yehova acitira cokoma onse;Ndi nsoni zokoma zace zigwera nchito zace zonse.

10. Nchito zanu zonse zidzakuyamikani, Yehova;Ndi okondedwa anu adzakulemekezani.

11. Adzanenera ulemerero wa ufumu wanu,Adzalankhulira mphamvu yanu;

12. Kudziwitsa ana a anthu zamphamvu zace,Ndi ulemerero waukuru wa ufumu wace.

13. Ufumu wanu ndiwo ufumu womka muyaya,Ndi kuweruza kwanu kufikira mibadwo yonse yonse.

14. Yehova agwiriziza onse akugwa,Naongoletsa onse owerama.

15. Maso a onse ayembekeza Inu;Ndipo muwapatsa cakudya cao m'nyengo zao.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 145