Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 145:13-21 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

13. Ufumu wanu ndiwo ufumu womka muyaya,Ndi kuweruza kwanu kufikira mibadwo yonse yonse.

14. Yehova agwiriziza onse akugwa,Naongoletsa onse owerama.

15. Maso a onse ayembekeza Inu;Ndipo muwapatsa cakudya cao m'nyengo zao.

16. Muniowetsa dzanja lanu,Nimukwaniritsira zamoyo zonse cokhumba cao.

17. Yehova ali wolungama m'njira zace zonse,Ndi wacifundo m'nchito zace zonse.

18. Yehova ali pafupi ndi onse akuitanira kwa Iye,Onse akuitanira kwa Iye m'coonadi.

19. Adzacita cokhumba iwo akumuopa;Nadzamva kupfuula kwao, nadzawapulumutsa.

20. Yehova asunga onse akukondana naye;Koma oipa onse adzawaononga.

21. Pakamwa panga padzanena cilemekezo ca Yehova;Ndi zinthu zonse zilemekeze dzina lace loyera ku nthawi za nthawi.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 145