Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 145:1-6 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndidzakukwezani Mulungu wanga, Mfumu;Ndipo ndidzalemekeza dzina lanu ku nthawi za nthawi.

2. Masiku onse ndidzakuyamikani;Ndi kulemekeza dzina lanu ku nthawi za nthawi.

3. Yehova ndi wamkulu, nayenera kulemekezedwa kwakukuru;Ndi ukulu wace ngwosasanthulika.

4. Mbadwo wina udzalemekezera nchito zanu mbadwo unzace,Ndipo udzalalikira zamphamvu zanu.

5. Ndidzalingalira ulemerero waukuru wa ulemu wanu,Ndi nchito zanu zodabwiza.

6. Ndipo adzanenera mphamvu za nchito zanu zoopsa;Ndi ukulu wanu ndidzaufotokozera.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 145