2. Pempherolanga liikike ngaticofukiza pamaso panu;Kukweza manja anga kuikike ngati nsembe ya madzulo.
3. Muike mdindo pakamwa panga, Yehova;Sungani pakhomo pa milomo yanga.
4. Mtima wanga usalinge ku cinthu coipa,Kucita nchito zoipaNdi anthu akucita zopanda pace;Ndipo ndisadye zankhuli zao.
5. Akandipanda munthu wolungama ndidzati ncifundo:Akandidzudzula, ndidzakuyesa mafuta a pamutu;Mutu wanga usakane:Pakuti pangakhale posautsidwa iwo ndidzawapempherera.
6. Oweruza ao anagwetseka pambali pa thanthwe;Nadzamva mau anga kuti ndiwo okondweretsa.
7. Mafupa athu amwazika pakamwa pa manda,Monga ngati akumba nanyimphula nthaka yapansi.
8. Pakuti maso anga apenya kwanu, Yehova Ambuye;Ndithawira kwa Inu; musataye moyowanga.
9. Mundisunge ndisagwe mumsampha anandicherawo,Ndisakodwe m'makwekwe a iwo ocita zopanda pace,
10. Oipa agwe pamodzi m'maukonde ao,Kufikira nditapitirira ine.