Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 138:2-7 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

2. Ndidzagwadira kuloza ku Kacisi wanu woyera,Ndi kuyamika dzina lanu,Cifukwa ca cifundo canu ndi coonadi canu;Popeza munakuzitsa mau anu koposa dzina lanu lonse.

3. Tsiku loitana ine, munandiyankha,Munandilimbitsa ndi mphamvu m'moyo mwanga.

4. Mafumu onse a pa dziko lapansi adzakuyamikani,Yehova, popeza adamva mau a pakamwa panu.

5. Ndipo adzayimbira njira za Yehova;Pakuti ulemerero wa Yehova ndi waukuru.

6. Angakhale Yehova ngwokwezeka, apenyanso wopepukayo;Koma wodzikuza amdziwira kutali.

7. Ndingakhale ndiyenda pakati pa nsautso, mudzandipatsa moyo;Mudzatambasula dzanja lanu pa mkwiyo wa adani anu,Ndipo dzanja lanu lamanja lidzandipulumutsa.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 138