Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 135:9-13 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

9. Anatumiza zizindikilo ndi zodabwiza pakati pako,Aigupto iwe, Pa Farao ndi pa omtumikira onse.

10. Ndiye amene anapanda amitundu ambiri.Napha mafumu amphamvu;

11. Sihoni mfumu ya Aamori,Ndi Ogi mfumu ya Basana,Ndi maufumu onse a Kanani:

12. Ndipo anapereka dziko lao likhale cosiyira,Cosiyira ca kwa Israyeli anthu ace.

13. Dzina lanu, Yehova, likhala kosatha;Cikumbukilo canu, Yehova, kufikira mibadwo mibadwo.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 135