8. Anapanda oyamba a Aigupto,Kuyambira munthu kufikira zoweta.
9. Anatumiza zizindikilo ndi zodabwiza pakati pako,Aigupto iwe, Pa Farao ndi pa omtumikira onse.
10. Ndiye amene anapanda amitundu ambiri.Napha mafumu amphamvu;
11. Sihoni mfumu ya Aamori,Ndi Ogi mfumu ya Basana,Ndi maufumu onse a Kanani:
12. Ndipo anapereka dziko lao likhale cosiyira,Cosiyira ca kwa Israyeli anthu ace.
13. Dzina lanu, Yehova, likhala kosatha;Cikumbukilo canu, Yehova, kufikira mibadwo mibadwo.
14. Pakuti Yehova adzaweruza anthu ace,Koma adzaleka atumiki ace.
15. Mafano a amitundu ndiwo siliva ndi golidi,Nchito ya manja a anthu.
16. Pakamwa ali napo koma osalankhula;Maso ali nao, koma osapenya;
17. Makutu ali nao, koma osamva;Inde, pakamwa pao palibe mpweya.
18. Akuwapanga adzafanana nao;Inde, onse akuwakhulupirira.
19. A nyumba ya Israyeli inu, lemekezani Yehova:A nyumba ya Aroni inu, lemekezani Yehova:
20. A nyumba ya Levi inu, lemekezani Yehova:Inu akuopa Yehova, lemekezani Yehova.