6. Ciri conse cimkonda Yehova acicita,Kumwamba ndi pa dziko lapansi, m'nyanja ndi mozama monse.
7. Akweza mitambo icokere ku malekezero a dziko lapansi;Ang'animitsa mphezi zidzetse mvula;Aturutsa mphepo mosungira mwace.
8. Anapanda oyamba a Aigupto,Kuyambira munthu kufikira zoweta.
9. Anatumiza zizindikilo ndi zodabwiza pakati pako,Aigupto iwe, Pa Farao ndi pa omtumikira onse.
10. Ndiye amene anapanda amitundu ambiri.Napha mafumu amphamvu;
11. Sihoni mfumu ya Aamori,Ndi Ogi mfumu ya Basana,Ndi maufumu onse a Kanani:
12. Ndipo anapereka dziko lao likhale cosiyira,Cosiyira ca kwa Israyeli anthu ace.
13. Dzina lanu, Yehova, likhala kosatha;Cikumbukilo canu, Yehova, kufikira mibadwo mibadwo.
14. Pakuti Yehova adzaweruza anthu ace,Koma adzaleka atumiki ace.
15. Mafano a amitundu ndiwo siliva ndi golidi,Nchito ya manja a anthu.