Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 135:1-14 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Haleluya;Lemekezani dzina la Yehova;Lemekezani inu atumiki a Yehova:

2. Inu akuimirira m'nyumba ya Yehova,M'mabwalo a nyumba ya Mulungu wathu.

3. Lemekezani Yehova; pakuti Yehova ndiye wabwino;Muyimbire zolemekeza dzina lace; pakuti nkokondweretsa kutero.

4. Pakuti Yehova anadzisankhira Yakobo,Israyeli, akhale cuma cace ceni ceni.

5. Pakuti ndidziwa kuti Yehova ndi wamkuru,Ndi Ambuye wathu aposa milungu yonse.

6. Ciri conse cimkonda Yehova acicita,Kumwamba ndi pa dziko lapansi, m'nyanja ndi mozama monse.

7. Akweza mitambo icokere ku malekezero a dziko lapansi;Ang'animitsa mphezi zidzetse mvula;Aturutsa mphepo mosungira mwace.

8. Anapanda oyamba a Aigupto,Kuyambira munthu kufikira zoweta.

9. Anatumiza zizindikilo ndi zodabwiza pakati pako,Aigupto iwe, Pa Farao ndi pa omtumikira onse.

10. Ndiye amene anapanda amitundu ambiri.Napha mafumu amphamvu;

11. Sihoni mfumu ya Aamori,Ndi Ogi mfumu ya Basana,Ndi maufumu onse a Kanani:

12. Ndipo anapereka dziko lao likhale cosiyira,Cosiyira ca kwa Israyeli anthu ace.

13. Dzina lanu, Yehova, likhala kosatha;Cikumbukilo canu, Yehova, kufikira mibadwo mibadwo.

14. Pakuti Yehova adzaweruza anthu ace,Koma adzaleka atumiki ace.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 135