Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 123:1-4 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndikweza maso anga kwa Inu,Kwa Inu wakukhala kumwamba.

2. Taonani, monga maso a anyamata ayang'anira dzanja la ambuye ao,Monga maso a adzakazi ayang'anira dzanja la mbuye wao wamkazi:Momwemo maso athu ayang'anira Yehova Mulungu wathu,Kufikira aticitira cifundo.

3. Muticitire cifundo, Yehova, muticitire cifundo;Pakuti takhuta kwambiri ndi mnyozo.

4. Moyo wathu wakhuta ndithuNdi kuseka kwa iwo osasowa kanthu,Ndi mnyozo wa odzikuza.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 123