1. Ndinakondwera m'mene ananena nane,Tiyeni ku nyumba ya Yehova.
2. Mapazi athu alinkuima M'zipata zanu, Yerusalemu.
3. Yerusalemu anamangidwaNgati mudzi woundana bwino:
4. Kumene akwerako mafuko, ndiwo mafuko a Yehova;Akhale mboni ya kwa Israyeli,Ayamike dzina la Yehova.
5. Pakuti pamenepo anaika mipando ya ciweruzo,Mipando ya nyumba ya Davide.
6. Mupempherere mtendere wa Yerusalemu;Akukonda inu adzaona phindu.
7. M'linga mwako mukhale mtendere,M'nyumba za mafumu mukhale phindu.
8. Cifukwa ca abale anga ndi mabwenzi anga,Ndidzanena tsopano, Mukhale mtendere mwa inu.