Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 121:3-8 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

3. Sadzalola phazi lako literereke:Iye amene akusunga sadzaodzera.

4. Taonani, wakusunga IsrayeaSadzaodzera kapena kugona.

5. Yehova ndiye wakukusunga;Yehova ndiye mthunzi wako wa ku dzanja lako lamanja.

6. Dzuwa silidzawamba usana,Mwezi sudzakupanda usiku.

7. Yehova adzakusunga kukucotsera zoipa ziri zonse;Adzasunga moyo wako.

8. Yehova adzasungira kuturuka kwako ndi kulowa kwako,Kuyambira tsopano kufikira nthawi zonse.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 121