Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 119:98-112 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

98. Malamulo anu andipatsa nzeru yakuposa adani anga;Pakuti akhala nane cikhalire.

99. Ndiri nayo nzeru yakuposa aphunzitsi anga onse;Pakuti ndilingalira mboni zanu.

100. Ndizindikira koposa okalambaPopeza ndinasunga malangizo anu.

101. Ndinaletsa mapazi anga njira iri yonse yoipa,Kuti ndisamalire mau anu.

102. Sindinapatukana nao maweruzo anu;Pakuti Inu munandiphunzitsa.

103. Mau anu azunadi powalawa ine!Koposa uci m'kamwa mwanga.

104. Malangizo anu andizindikiritsa;Cifukwa cace ndidana nao mayendedwe onse acinyengo,

105. Mau anu ndiwo nyali ya ku mapazi anga,Ndi kuunika kwa panjira panga,

106. Ndinalumbira, ndipo ndinatsimikiza mtima,Kuti ndidzasamalira maweruzo anu olungama.

107. Ndazunzika kwambiri:Ndipatseni moyo, Yehova, monga mwa mau anu.

108. Landirani, Yehova, zopereka zaufulu za pakamwa panga,Ndipo ndiphunzitseni maweruzo anu.

109. Moyo wanga ukhala m'dzanja langa cikhalire;Koma sindiiwala cilamulo canu.

110. Oipa anandichera msampha;Koma sindinasokera m'malangizo anu.

111. Ndinalandira mboni zanu zikhale colandira cosatha;Pakuti ndizo zokondweretsa mtima wanga.

112. Ndinalingitsa mtima wanga ucite malemba anu,Kosatha, kufikira cimatiziro.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 119