Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 119:95-104 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

95. Oipa anandilalira kundiononga;Koma ndizindikira mboni zanu.

96. Ndinapenya malekezero ace a ungwiro wonse;Koma lamulo lanu ndi lotakasuka ndithu.

97. Ha! Ndikondadi cilamulo canu;Ndilingiriramo ine tsiku lonse.

98. Malamulo anu andipatsa nzeru yakuposa adani anga;Pakuti akhala nane cikhalire.

99. Ndiri nayo nzeru yakuposa aphunzitsi anga onse;Pakuti ndilingalira mboni zanu.

100. Ndizindikira koposa okalambaPopeza ndinasunga malangizo anu.

101. Ndinaletsa mapazi anga njira iri yonse yoipa,Kuti ndisamalire mau anu.

102. Sindinapatukana nao maweruzo anu;Pakuti Inu munandiphunzitsa.

103. Mau anu azunadi powalawa ine!Koposa uci m'kamwa mwanga.

104. Malangizo anu andizindikiritsa;Cifukwa cace ndidana nao mayendedwe onse acinyengo,

Werengani mutu wathunthu Masalmo 119