Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 119:94-108 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

94. Ine ndine wanu, ndipulumutseniPakuti ndinafuna malangizo anu.

95. Oipa anandilalira kundiononga;Koma ndizindikira mboni zanu.

96. Ndinapenya malekezero ace a ungwiro wonse;Koma lamulo lanu ndi lotakasuka ndithu.

97. Ha! Ndikondadi cilamulo canu;Ndilingiriramo ine tsiku lonse.

98. Malamulo anu andipatsa nzeru yakuposa adani anga;Pakuti akhala nane cikhalire.

99. Ndiri nayo nzeru yakuposa aphunzitsi anga onse;Pakuti ndilingalira mboni zanu.

100. Ndizindikira koposa okalambaPopeza ndinasunga malangizo anu.

101. Ndinaletsa mapazi anga njira iri yonse yoipa,Kuti ndisamalire mau anu.

102. Sindinapatukana nao maweruzo anu;Pakuti Inu munandiphunzitsa.

103. Mau anu azunadi powalawa ine!Koposa uci m'kamwa mwanga.

104. Malangizo anu andizindikiritsa;Cifukwa cace ndidana nao mayendedwe onse acinyengo,

105. Mau anu ndiwo nyali ya ku mapazi anga,Ndi kuunika kwa panjira panga,

106. Ndinalumbira, ndipo ndinatsimikiza mtima,Kuti ndidzasamalira maweruzo anu olungama.

107. Ndazunzika kwambiri:Ndipatseni moyo, Yehova, monga mwa mau anu.

108. Landirani, Yehova, zopereka zaufulu za pakamwa panga,Ndipo ndiphunzitseni maweruzo anu.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 119