85. Odzikuza anandikumbira mbuna,Ndiwo osasamalira cilamulo canu.
86. Malamulo anu onse ngokhulupirika;Andilondola nalo bodza; ndithandizeni.
87. Akadandithera pa dziko lapansi; Koma ine sindinasiya malangizo anu.
88. Mundipatse moyo monga mwa cifundo canu;Ndipo ndidzasamalira mboni ya pakamwa panu,
89. Mau anu aikika kumwamba,Kosatha, Yehova.
90. Cikhulupiriko canu cifikira mibadwo mibadwo;Munakhazikitsa dziko lapansi, ndipo likhalitsa.
91. Kunena za maweruzo anu alimbikira kufikira lero;Pakuti onsewa ndiwo atumiki anu.
92. Cilamulo canu cikadapanda kukhala cikondweretso canga,Ndikadatayika m'kuzunzika kwanga.
93. Sindidzaiwala malangizo anu nthawi zonse;Popeza munandipatsa nao moyo.
94. Ine ndine wanu, ndipulumutseniPakuti ndinafuna malangizo anu.
95. Oipa anandilalira kundiononga;Koma ndizindikira mboni zanu.