79. Iwo akuopa Inu abwere kwa ine,Ndipo adzadziwa mboni zanu.
80. Mtima wanga ukhale wangwiro m'malemba anu;Kuti ndisacite manyazi.
81. Moyo wanga unakomoka ndi kukhumba cipulumutso canu:Ndinayembekezera mau anu.
82. Maso anga anatha mphamvu ndi kukhumba mau anu,Ndikuti, Mudzanditonthoza liti?
83. Popeza ndakhala ngati thumba lofukirira;Koma sindiiwala malemba anu.
84. Masiku a mtumiki wanu ndiwo angati?Mudzaweruza liti iwo akundilondola koipa?
85. Odzikuza anandikumbira mbuna,Ndiwo osasamalira cilamulo canu.
86. Malamulo anu onse ngokhulupirika;Andilondola nalo bodza; ndithandizeni.
87. Akadandithera pa dziko lapansi; Koma ine sindinasiya malangizo anu.
88. Mundipatse moyo monga mwa cifundo canu;Ndipo ndidzasamalira mboni ya pakamwa panu,
89. Mau anu aikika kumwamba,Kosatha, Yehova.