Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 119:77-90 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

77. Nsoni zokoma zanu zindidzere, kuti ndikhale ndi moyo;Popeza cilamulo canu cindikondweretsa.

78. Odzikuza acite manyazi, popeza anandicitira monyenga ndi bodza:Koma ine ndidzalingalira malangizo anu.

79. Iwo akuopa Inu abwere kwa ine,Ndipo adzadziwa mboni zanu.

80. Mtima wanga ukhale wangwiro m'malemba anu;Kuti ndisacite manyazi.

81. Moyo wanga unakomoka ndi kukhumba cipulumutso canu:Ndinayembekezera mau anu.

82. Maso anga anatha mphamvu ndi kukhumba mau anu,Ndikuti, Mudzanditonthoza liti?

83. Popeza ndakhala ngati thumba lofukirira;Koma sindiiwala malemba anu.

84. Masiku a mtumiki wanu ndiwo angati?Mudzaweruza liti iwo akundilondola koipa?

85. Odzikuza anandikumbira mbuna,Ndiwo osasamalira cilamulo canu.

86. Malamulo anu onse ngokhulupirika;Andilondola nalo bodza; ndithandizeni.

87. Akadandithera pa dziko lapansi; Koma ine sindinasiya malangizo anu.

88. Mundipatse moyo monga mwa cifundo canu;Ndipo ndidzasamalira mboni ya pakamwa panu,

89. Mau anu aikika kumwamba,Kosatha, Yehova.

90. Cikhulupiriko canu cifikira mibadwo mibadwo;Munakhazikitsa dziko lapansi, ndipo likhalitsa.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 119