Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 119:74-79 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

74. Iwo amene akuopani adzandiona ine nadzakondwera;Popeza ndayembekezera mau anu;

75. Ndidziwa kuti maweruzo anu ndiwo olungama, Yehova,Ndi kuti munandizunza ine mokhulupirika.

76. Cifundo canu cikhaletu cakunditonthoza, ndikupemphani,Monga mwa mau anu kwa mtumiki wanu.

77. Nsoni zokoma zanu zindidzere, kuti ndikhale ndi moyo;Popeza cilamulo canu cindikondweretsa.

78. Odzikuza acite manyazi, popeza anandicitira monyenga ndi bodza:Koma ine ndidzalingalira malangizo anu.

79. Iwo akuopa Inu abwere kwa ine,Ndipo adzadziwa mboni zanu.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 119