Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 119:66-85 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

66. Mundiphunzitse cisiyanitso ndi nzeru;Pakuti ndinakhulupirira malamulo anu.

67. Ndisanazunzidwe ndinasokera; Koma tsopano ndisamalira mau anu.

68. Inu ndinu wabwino, ndi wakucita zabwino;Mundiphunzitse malemba anu.

69. Odzikuza anandipangira bodza:Ndidzasunga malangizo anu ndi mtima wanga wonse.

70. Mtima wao unona ngati mafuta;Koma ine ndikondwera naco cilamulo canu.

71. Kundikomera kuti ndinazunzidwa;Kuti ndiphunzire malemba anu.

72. Cilamulo ca pakamwa panu cindikomeraKoposa golidi ndi siliva zikwi zikwi.

73. Manja anu anandilenga nandiumba;Mundizindikiritse, kuti ndiphunzire malemba anu.

74. Iwo amene akuopani adzandiona ine nadzakondwera;Popeza ndayembekezera mau anu;

75. Ndidziwa kuti maweruzo anu ndiwo olungama, Yehova,Ndi kuti munandizunza ine mokhulupirika.

76. Cifundo canu cikhaletu cakunditonthoza, ndikupemphani,Monga mwa mau anu kwa mtumiki wanu.

77. Nsoni zokoma zanu zindidzere, kuti ndikhale ndi moyo;Popeza cilamulo canu cindikondweretsa.

78. Odzikuza acite manyazi, popeza anandicitira monyenga ndi bodza:Koma ine ndidzalingalira malangizo anu.

79. Iwo akuopa Inu abwere kwa ine,Ndipo adzadziwa mboni zanu.

80. Mtima wanga ukhale wangwiro m'malemba anu;Kuti ndisacite manyazi.

81. Moyo wanga unakomoka ndi kukhumba cipulumutso canu:Ndinayembekezera mau anu.

82. Maso anga anatha mphamvu ndi kukhumba mau anu,Ndikuti, Mudzanditonthoza liti?

83. Popeza ndakhala ngati thumba lofukirira;Koma sindiiwala malemba anu.

84. Masiku a mtumiki wanu ndiwo angati?Mudzaweruza liti iwo akundilondola koipa?

85. Odzikuza anandikumbira mbuna,Ndiwo osasamalira cilamulo canu.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 119