Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 119:62-69 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

62. Pakati pa usiku ndidzauka kukuyamikaniCifukwa ca maweruzo anu olungama.

63. Ine ndine wakuyanjana nao onse akukuopani,Ndi iwo akusamalira malangizo anu.

64. Dziko lapansi lidzala naco cifundo canu, Yehova;Mundiphunzitse malemba anu.

65. Munacitira mtumiki wanu cokoma, Yehova,Monga mwa mau anu.

66. Mundiphunzitse cisiyanitso ndi nzeru;Pakuti ndinakhulupirira malamulo anu.

67. Ndisanazunzidwe ndinasokera; Koma tsopano ndisamalira mau anu.

68. Inu ndinu wabwino, ndi wakucita zabwino;Mundiphunzitse malemba anu.

69. Odzikuza anandipangira bodza:Ndidzasunga malangizo anu ndi mtima wanga wonse.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 119