Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 119:59-75 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

59. Ndinaganizira njira zanga,Ndipo ndinabweza mapazi anga atsate mboni zanu.

60. Ndinafulumira, osacedwa,Kusamalira malamulo anu.

61. Anandikulunga nazo zingwe za oipa;Koma sindinaiwala cilamulo canu.

62. Pakati pa usiku ndidzauka kukuyamikaniCifukwa ca maweruzo anu olungama.

63. Ine ndine wakuyanjana nao onse akukuopani,Ndi iwo akusamalira malangizo anu.

64. Dziko lapansi lidzala naco cifundo canu, Yehova;Mundiphunzitse malemba anu.

65. Munacitira mtumiki wanu cokoma, Yehova,Monga mwa mau anu.

66. Mundiphunzitse cisiyanitso ndi nzeru;Pakuti ndinakhulupirira malamulo anu.

67. Ndisanazunzidwe ndinasokera; Koma tsopano ndisamalira mau anu.

68. Inu ndinu wabwino, ndi wakucita zabwino;Mundiphunzitse malemba anu.

69. Odzikuza anandipangira bodza:Ndidzasunga malangizo anu ndi mtima wanga wonse.

70. Mtima wao unona ngati mafuta;Koma ine ndikondwera naco cilamulo canu.

71. Kundikomera kuti ndinazunzidwa;Kuti ndiphunzire malemba anu.

72. Cilamulo ca pakamwa panu cindikomeraKoposa golidi ndi siliva zikwi zikwi.

73. Manja anu anandilenga nandiumba;Mundizindikiritse, kuti ndiphunzire malemba anu.

74. Iwo amene akuopani adzandiona ine nadzakondwera;Popeza ndayembekezera mau anu;

75. Ndidziwa kuti maweruzo anu ndiwo olungama, Yehova,Ndi kuti munandizunza ine mokhulupirika.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 119