Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 119:59-65 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

59. Ndinaganizira njira zanga,Ndipo ndinabweza mapazi anga atsate mboni zanu.

60. Ndinafulumira, osacedwa,Kusamalira malamulo anu.

61. Anandikulunga nazo zingwe za oipa;Koma sindinaiwala cilamulo canu.

62. Pakati pa usiku ndidzauka kukuyamikaniCifukwa ca maweruzo anu olungama.

63. Ine ndine wakuyanjana nao onse akukuopani,Ndi iwo akusamalira malangizo anu.

64. Dziko lapansi lidzala naco cifundo canu, Yehova;Mundiphunzitse malemba anu.

65. Munacitira mtumiki wanu cokoma, Yehova,Monga mwa mau anu.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 119