Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 119:54-66 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

54. Malemba anu anakhala nyimbo zangaM'nyumba ya ulendo wanga,

55. Usiku ndinakumbukila dzina lanu, Yehova,Ndipo ndinasamalira cilamulo canu.

56. Ici ndinali naco,Popeza ndinasunga malangizo anu.

57. Yehova ndiye gawo langa:Ndinati ndidzasunga mau anu.

58. Ndinapemba pankhope panu ndi mtima wanga wonse:Mundicitire cifundo monga mwa mau anu.

59. Ndinaganizira njira zanga,Ndipo ndinabweza mapazi anga atsate mboni zanu.

60. Ndinafulumira, osacedwa,Kusamalira malamulo anu.

61. Anandikulunga nazo zingwe za oipa;Koma sindinaiwala cilamulo canu.

62. Pakati pa usiku ndidzauka kukuyamikaniCifukwa ca maweruzo anu olungama.

63. Ine ndine wakuyanjana nao onse akukuopani,Ndi iwo akusamalira malangizo anu.

64. Dziko lapansi lidzala naco cifundo canu, Yehova;Mundiphunzitse malemba anu.

65. Munacitira mtumiki wanu cokoma, Yehova,Monga mwa mau anu.

66. Mundiphunzitse cisiyanitso ndi nzeru;Pakuti ndinakhulupirira malamulo anu.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 119