45. Ndipo ndidzayenda mwaufulu;Popeza ndinafuna malangizo anu.
46. Ndidzalankhulanso za umboni wanu pamaso pa mafumu,Osacitapo manyazi.
47. Ndipo ndidzadzikondweretsa nao malamulo anu,Amene ndiwakonda.
48. Ndidzakwezanso manja anga ku malamulo anu, amene ndiwakonda;Ndipo ndidzalingalira pa malemba anu.
49. Kumbukilani mau a kwa mtumiki wanu,Amene munandiyembekezetsa nao.