Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 119:45-49 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

45. Ndipo ndidzayenda mwaufulu;Popeza ndinafuna malangizo anu.

46. Ndidzalankhulanso za umboni wanu pamaso pa mafumu,Osacitapo manyazi.

47. Ndipo ndidzadzikondweretsa nao malamulo anu,Amene ndiwakonda.

48. Ndidzakwezanso manja anga ku malamulo anu, amene ndiwakonda;Ndipo ndidzalingalira pa malemba anu.

49. Kumbukilani mau a kwa mtumiki wanu,Amene munandiyembekezetsa nao.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 119