Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 119:44-52 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

44. Potero ndidzasamalira malamulo anu cisamalireKu nthawi za nthawi.

45. Ndipo ndidzayenda mwaufulu;Popeza ndinafuna malangizo anu.

46. Ndidzalankhulanso za umboni wanu pamaso pa mafumu,Osacitapo manyazi.

47. Ndipo ndidzadzikondweretsa nao malamulo anu,Amene ndiwakonda.

48. Ndidzakwezanso manja anga ku malamulo anu, amene ndiwakonda;Ndipo ndidzalingalira pa malemba anu.

49. Kumbukilani mau a kwa mtumiki wanu,Amene munandiyembekezetsa nao.

50. Citonthozo canga m'kuzunzika kwanga ndi ici;Pakuti mau anu anandipatsa moyo.

51. Odzikuza anandinyoza kwambiri:Koma sindinapatukanso naco cilamulo canu.

52. Ndinakumbukila maweruzo anu kuyambira kale, Yehova,Ndipo ndinadzitonthoza.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 119